Yemwe adabweretsa mwambi woti kunena kwa ndithe ndithe nanthambwe adadzitengera, adalinga ataona kuti tsiku lina woyimba Duncan Zgambo, wotchuka ndi dzina loti Gwamba, adzadzilasa yekha pochita lonjezo losakwaniritsidwa.
Chatsitsa dzaye nchakuti pa 21 September, 2024, Gwamba yemwe omunyadira amamutcha GOAT, adali ndi mphwando la nyimbo pa bwalo la Civo munzinda wa Lilongwe lomwe ankalitcha “The Best of Gwamba Concert.”
Pa tsikuli kudali kubwira fumbi, pomwe oyimba ngati Focalistic wa m’dziko la South Africa komaso ena a pampanje pano, adadumphitsa anthu ma sipika.
Koma poti chuluke chuluke ndi wa njuchi umanena iyo yakulasa mbola, tsikuli linali la wamba makamaka kwa anthu okonda chamba, inde chamba cha lege poti utsi pa Civo sunafuke.
Gwamba sanaitane gulu la Black Missionaries, chomwe chinali chibwana cha mchombo lende. Ambiri okonda chamba cha lege sizidawakonde.
Patapita miyezi iwiri phwandoli chichitikireni, pa 5 November, 2024 Gwamba naye, adavomereza kuti kusatenga Ma Blacks idali “mistake” ndipo adalonjeza kuti sadzapangaso, mawu omwe lero amubwererera.
“Mkulu wanga! Ndamuuza kuti mistake yopanga show nkusiya ma Blacks sizachitikanso!! Ndasiya chibwana chimenecho,” adatelo Gwamba. “Ndakula ndasiya chibwana.”
Mawuwa amulasa woyimbayu kaamba koti phwando lotchedwa “Landlord Pa Kwawo” lomwe anachititsaso Loweruka lapitali pa bwalo la Bingu, kunalibe Ma Blacks.
Izi zapangitsa anthu kukafukula zomwe Gwamba adalemba pa 5 November, 2024 zija zolonjeza kuti sadzawasiyaso Ma Blacks, ndipo ambiri ati anali odabwa kuti gulu la chamba cha legeli silinaitanidweso.
“Ndiye apa simunawasiyaso. Palibwino kusiya onse aja ndikutenga ma blacks okha,” iyo idali ndemanga ya Ma Jamilah, yomwe siikusiyana ndi zomwe Chimzie Mmadih adalemba poti, “show ikhala bwanji yopanda ma blacks?”
Anthu ena akumbutsa woyimbayu kuti asamakomedwe polankhula. ” Osamatha mawu,” adatelo Achina Shame, pomwe Vitu Chisi adangoti, “nthawi mkachitsiru.”
Naye Elosie Mahau adakumbutsa “Landlord” kuti azikwanikitsa lonjezo ponena kuti intaneti siimaiwala munthu akalankhula.
Koma ngakhale zili choncho, anthu ena ati phwando la Loweruka linali kale bwino kotero Ma Blacks samafunikirako.
“Ma blacks achaniso m’mene zinaliri muja hhhh,” Violet Vionnah Violetta Kamwendo.
Facts Only
* Gwamba held a concert on September 21, 2024, at the Civo venue in Lilongwe.
* The concert included music from South Africa and Focalistic.
* Gwamba later stated that the arrangement was a mistake and demanded the removal of the association with Ma Blacks.
* A subsequent performance, "Landlord Pa Kwawo," was scheduled at Bingu and included Ma Blacks.
* Some participants suggested that the show could proceed without Ma Blacks.
* Achina Shame requested silence regarding the topic until the time was right.
* Elosie Mahau referenced the internet's inability to accommodate lengthy discussions.
* Violet Vionnah Violetta Kamwendo stated that Ma Blacks were "already there."
Executive Summary
Full Take
Sentinel — Human
The text reads like a transcription or highly narrative summary of an oral discussion, characterized by conversational flow and embedded anecdotal evidence rather than structured journalistic exposition.
